Mlomo wanga
Sudzandiphurira ngozi Kodi?
Nchiani ukambazi?
Pali anthu akulu akulu Pano
Wakuuza ndani?
Abusa sanamvetu izi
Iwe waziba kuti?
Mbiyang'ambe ya mudzi
Ludzu lako naliwona
Kumtsinje wabibida
Iwe ndikabwerebwere
Iwe simlendo pamudzi Pano
Usandiuze wadza kamlomo wakuthwa
Sukadakhala chete kodi?
Palitu aneneri Pano
Nchiani ukambachi?
Oh Maine! Mlomo wanga
Wandiputilanji?
Oh Maine! Mlomo wanga
Ndilire bwanji?
Ndikudziwa mtima umawawa
Komabe ukanakhala chete
Ukambazi ulaula mtundu
This poem has not been translated into any other language yet.
I would like to translate this poem